Psalms 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga ku mapiri;
kodi thandizo langa limachokera kuti?
2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola kuti phazi lako literereke;
Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4Taonani, Iye amene amasunga Israeli
sadzawodzera kapena kugona.

5Yehova ndiye amene amakusunga;
Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,
kapena mwezi nthawi ya usiku.

7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;
adzasunga moyo wako.
8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Copyright information for NyaCCL